< Masalimo 59 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Přednímu z kantorů, jako: Nevyhlazujž, Davidův žalm zlatý, když poslal Saul, aby střehouc domu, zabili ho. Vytrhni mne od nepřátel mých, Bože můj; před těmi, kteříž povstávají proti mně, bezpečna mne učiň.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Vytrhni mne od těch, kteříž páší nepravost, a od mužů vražedlných zachovej mne.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
Neb aj, zálohy činí duši mé, sbírají se proti mně mocní, bez mého provinění a bez hříchu mého, ó Hospodine.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Beze vší mé nepravosti sbíhají se, a strojí; povstaniž mně vstříc, a popatř.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Sám ty, Hospodine Bože zástupů, Bože Izraelský, prociť, abys navštívil všecky národy, aniž se smilovávej nad kterým z těch převrácenců nešlechetných. (Sélah)
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Navracejí se k večerou, štěkají jako psi, a běhají okolo města.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Aj, coť vynášejí ústy svými! Mečové jsou ve rtech jejich, nebo říkají: Zdaliž kdo slyší?
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
Ale ty, Hospodine, směješ se jim, posmíváš se všechněm národům.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
Když on moc provozuje, na tebe pozor míti budu, nebo ty, Bože, jsi hrad můj vysoký.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
Bůh mně milosrdný předejdeť mne, Bůh dá mi viděti pomstu nad nepřátely mými.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Nezbijej jich, aby nezapomněl lid můj, ale zmítej jimi mocí svou, a sházej je, pavézo naše, ó Pane.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
Hřích úst svých, slova rtů svých, (postiženi jsouce v pýše své, pro prokletí a chřadnutí), ať vypravují.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Zahlaď v prchlivosti, zahlaď je, ať jich není, ať poznají, že Bůh panuje v Jákobovi i do končin země. (Sélah)
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
I nechažť se pak zase navracejí k večerou, štěkají jako psi, a běhají okolo města.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
Nechať těkají, a potravy hledají, však hladovití jsouce, uložiti se musejí.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
Já pak zpívati budu o síle tvé, hned z jitra hlasitě slaviti budu milosrdenství tvé, nebo jsi byl hrad můj vysoký, a útočiště v den ssoužení mého.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
A posilen jsa, žalmy tobě zpívati budu; nebo jsi Bůh, vysoký hrad můj, Bůh mně milosrdný.

< Masalimo 59 >