< Masalimo 59 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
За първия певец, по Не Разорявай. Песен на Давида, когато Саул прати стражи да пазят къщата, в която бе Давид, за да го убият. Избави ме от неприятелите ми, Боже мой; Тури ме на високо от ония, които се повдигат против мене.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Избави ме от ония, които вършат беззаконие, И спаси ме от кръвопийци.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
Защото, ето, причакват за да уловят душата ми; Силните се събират против мене, Не за мое престъпление, Господи, нито за мой грях.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Без да има в мене вина тичат и се готвят; Събуди се да ме посрещнеш и виж.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Ти, Господи Боже на силите, Боже Израилев, Стани за да посетиш всички народи; Да не покажеш милост към никого от нечестивите престъпници. (Села)
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Вечер се връщат, Вият като кучета и обикалят града.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Ето, те бълват думи с устата си; Мечове има в устните им, Понеже, думат те: Кой слуша?
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
Но, Ти Господи, ще им се присмееш, Ще се поругаеш на всички тия народи.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
О Сило моя, на Тебе ще се надея. Защото Бог ми е крепост.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
Милостивият мой Бог ще ме предвари; Бог ще ме удостои да видя повалянето на ония, които ме причакват.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Да ги не убиеш, да не би да забравят това моите люде; Разпръсни ги със силата Си. И свели ги, Господи, защитниче наш.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
Поради греха на устата си, поради думите на устните си, Нека бъдат уловени в гордостта си, Също и поради клетвата и лъжата що говорят.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Довърши го с гняв, довърши ги да ги няма вече, И нека се научат, че Бог господарува в Якова И до краищата на земята. (Села)
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
Нека се връщат вечер, Нека вият като кучета, и нека обикалят града;
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
Нека се скитат за храна; И ако не се настанят, нека прекарат нощта не наситени.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
А аз ще пия за Твоята сила, Да! на ранина високо ще славословя Твоята милост; Защото Ти си ме станал крепост И прибежище в деня на бедствието ми.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
О Сило моя, на Тебе ще пея хваление. Защото Ти, Боже, милостиви мой Бог, Си крепост моя.

< Masalimo 59 >