< Masalimo 59 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Na Gode! Nama ha lai dunu ilia na fane legesa: besa: le, Dia na gaga: ma! Nama ha lai dunu da nama doagala: be amoga na gaga: ma!
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Amo wadela: i hamosu dunu ili na fane legesa: besa: le, na gaga: ma.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
Ba: ma! Ilia da na fane legemusa: oulela. Dodona: gi dunu ilia da na fane legemusa: gegedosa. Bai na wadela: i hou hamoiba: le, hame amaha.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Hina Gode! Na da giadofale hame hamoi. Be ilia da hedolowane na doagala: musa: oulelefula.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Hina Gode Bagadedafa! Na fidimusa: wale gadoma! Isala: ili Gode! Disu ba: ma! Walegadole, wadela: i hamosu dunuma se bidi ima! Wadela: i hohonosu dunu ilima mae asigima!
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
Ilia da wa: mega gesenebe agoane, daeya bu misini, moilai bai bagade ganodini gegesenesa ahoa.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Ilia odagia gadesa amola magagisu hou amo nabima! Ilia lafi ganodini gona: su da gegesu gobihei agoai gala. Be ilia hamobe amo da enoga hame nabahayale, ilisu dawa: sa.
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
Be Hina Gode! Di da iliba: le ousa! Di da wadela: i hamosu dunu huluane amoba: le oufesega: sa.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
Gode! Di da gasa bagadeba: le, na da hahawane bagade Dia hou dafawaneyale dawa: sa. Gode! Di da na wamoaligisu sogebi gala.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
Na Gode da nama asigisa. Amola E da nama fidimusa: misunu. E da na siga ba: ma: ne, nama ha lai dunu ili hasalimu.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Gode! Na fi dunu ilia Dia hou gogolesa: besa: le, nama ha lai dunu mae fane lelegema. Be ninia Hina Gode! Ninia Gaga: su! Dia gasaga ili afagogolesili, ili hasalima.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
Ilia wadela: i hou da ilia lafi gadofo da: iya diala. Ilia sia: be huluanedafa da wadela: i sia: fawane sia: sa. Ilila: gasa hidale hou hamobeba: le, ilia da fedege agoane saniga sa: i dagoi ba: mu da defea.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Ilia da wadela: i sia: amola ogogosu bagade sia: beba: le, Dia ougi hou amoga ili dafawanedafa gugunufinisima. Amasea, dunu huluanedafa da Gode da Isala: ili fi dunu amola osobo bagade fifi asi gala dunu huluanedafa ili ouligisa, amo dawa: mu.
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
Nama ha lai dunu, ilia da wa: mega gesenebe agoane, daeya bu misini, moilai ganodini gegesenesa ahoa.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
Ilia da wa: me ha: i manu hogola labe amola ha: i manu hame galea gaga: nosa labe, agoai gala.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
Be na da Dia gasa dawa: beba: le, gesami hea: mu. Hahabe huluanedafa, na da Dia mae fisili asigidafa hou amoma nodoma: ne, gesami ha: gidafa hea: mu. Di da na bidi hamosu ba: i eso amoga, na wamoaligisu sogebi dialebe ba: i.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
Na Gaga: sudafa! Na da Dima nodomu! Na wamoaligisu sogebi da Gode! Amola Gode da nama hahawane dogolegesu gala.

< Masalimo 59 >