< Masalimo 58 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Isibili likhuluma okulungileyo yini, babusi? Lehlulela ngokuqonda yini, madodana abantu?
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Yebo, enhliziyweni lenza okubi, lilinganisa udlakela lwezandla zenu emhlabeni.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Ababi baba ngabemzini kusukela esiswini, bayaduha kusukela esizalweni, beqamba amanga.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Ubuhlungu babo bunjengobuhlungu benyoka, banjengebululu elingezwayo, elivimba indlebe yalo,
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
ukuze lingezwa ilizwi labalumbi abalumba amalumbo ngokuhlakanipha.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
Nkulunkulu, yephula amazinyo abo emlonyeni wabo, uphohloze amazinyo emihlathi yamabhongo ezilwane, Nkosi.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Kabancibilike njengamanzi agelezayo; nxa egobisa idandili lakhe ukutshoka umtshoko wakhe, babe njengabaqunywe iziqa.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
Kahambe njengomnenke oncibilikayo; njengomphunzo owesifazana, kabangaliboni ilanga.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Imbiza zenu zingakaluzwa ukhuni lwameva, uzabaphephula esiphephweni njengabaphilayo njengentukuthelweni.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
Olungileyo uzathokoza lapho ebona impindiselo, uzageza inyawo zakhe egazini lomubi.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
Ukuze umuntu athi: Impela ukhona umvuzo wolungileyo; impela ukhona uNkulunkulu owahlulela emhlabeni.

< Masalimo 58 >