< Masalimo 58 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Ya Mukulu wa Bayimbi. Ku ddoboozi, “Tozikiriza.” Zabbuli ya Dawudi. Ddala mwogera eby’amazima oba musirika busirisi? Abaana b’abantu mubasalira emisango mu bwenkanya?
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Nedda, mutegeka ebitali bya bwenkanya mu mitima gyammwe; era bye mukola bireeta obwegugungo mu nsi.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Abakola ebibi bakyama nga baakazaalibwa, bava mu lubuto nga balina ekibi, era bakula boogera bya bulimba.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Balina obusagwa ng’obw’omusota; bali ng’enswera etawulira ezibikira amatu gaayo;
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
n’etawulira na luyimba lwa mukugu agisendasenda okugikwata.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
Ayi Katonda, menya amannyo gaabwe; owangulemu amannyo g’empologoma zino, Ayi Mukama.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Leka babule ng’amazzi agakulukuta ne gagenda. Bwe banaanuula omutego, leka obusaale bwabwe bwe balasa bufufuggale.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
Babe ng’ekkovu erisaanuukira mu lugendo lwalyo. Babe ng’omwana azaaliddwa ng’afudde, ataliraba ku njuba!
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Nga n’entamu tennabuguma, alibayerawo n’obusungu obungi nga kibuyaga ow’amaanyi ennyo.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
Omutuukirivu alisanyuka ng’alabye bamuwalanidde eggwanga, olwo n’ebigere bye ne bisaabaana omusaayi ogw’abakola ebibi.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
Awo abantu bonna balyogera nti, “Ddala, abatuukirivu balwanirirwa. Ddala waliwo Katonda alamula mu bwenkanya ku nsi.”

< Masalimo 58 >