< Masalimo 58 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Jusqu'à la Fin, avec cette inscription de David: Ne détruis pas. O fils des hommes, si vous parlez sincèrement de la justice, jugez donc avec droiture.
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Car vous faites en votre cœur des iniquités sur la terre, et vos mains trament l'injustice.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Dès le sein de leur mère, les pécheurs ont dévié; à peine hors de ses entrailles, ils se sont égarés; ils ont dit des mensonges.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Leur colère est comme le venin du serpent, ou du sourd aspic, dont les oreilles sont bouchées,
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
Qui n'entendra point la voix des enchanteurs, et résistera aux charmes les plus subtils.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
Dieu leur a brisé les dents dans la bouche; le Seigneur a broyé la mâchoire des lions.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Ils s'écouleront comme un flot qui passe; le Seigneur tiendra son arc tendu contre eux, jusqu'à ce qu'ils aient péri.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
Ils seront réduits à rien, comme la cire qui se fond; le feu est tombé sur eux, ils n'ont plus vu le soleil.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Avant que vos épines approchent de la hauteur d'un arbrisseau, le Seigneur vous dévorera même pleins de vie, dans l'excès de sa colère.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
Le juste se réjouira, lorsqu'il verra la punition des impies; il se lavera les mains dans le sang des pécheurs.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
Et l'on dira: Puisqu'il y a des fruits pour les justes, il est donc un Dieu qui les juge sur la terre.