< Masalimo 58 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
`In Ebreu thus, To victorie; `lese thou not the swete song, ether the semely salm, of Dauid. `In Jeroms translacioun thus, To the ouercomere, that thou lese not Dauid, meke and simple. Forsothe if ye speken riytfulnesse verili; ye sones of men, deme riytfuli.
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
For in herte ye worchen wickidnesse in erthe; youre hondis maken redi vnriytfulnessis.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Synneris weren maad aliens fro the wombe; thei erriden fro the wombe, thei spaken false thingis.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Woodnesse is to hem, bi the licnesse of a serpent; as of a deef snake, and stoppynge hise eeris.
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
Which schal not here the vois of charmeris; and of a venym makere charmynge wiseli.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
God schal al to-breke the teeth of hem in her mouth; the Lord schal breke togidere the greet teeth of liouns.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Thei schulen come to nouyt, as water rennynge awei; he bente his bouwe, til thei ben maad sijk.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
As wexe that fletith awei, thei schulen be takun awei; fier felle aboue, and thei siyen not the sunne.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Bifore that youre thornes vndurstoden the ramne; he swolewith hem so in ire, as lyuynge men.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
The iust man schal be glad, whanne he schal se veniaunce; he schal waische hise hondis in the blood of a synner.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
And a man schal seie treuli, For fruyt is to a iust man; treuli God is demynge hem in erthe.

< Masalimo 58 >