< Masalimo 58 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
Do you indeed speak righteousness, O congregation? do you judge uprightly, O you sons of men?
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
Yes, in heart you work wickedness; you weigh the violence of your hands in the earth.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
The wicked are estranged from the womb: they go astray as soon as they be born, speaking lies.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Their poison is like the poison of a serpent: they are like the deaf adder that stops her ear;
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
Which will not listen to the voice of charmers, charming never so wisely.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
Break their teeth, O God, in their mouth: break out the great teeth of the young lions, O LORD.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
Let them melt away as waters which run continually: when he bends his bow to shoot his arrows, let them be as cut in pieces.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
As a snail which melts, let every one of them pass away: like the untimely birth of a woman, that they may not see the sun.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Before your pots can feel the thorns, he shall take them away as with a whirlwind, both living, and in his wrath.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
The righteous shall rejoice when he sees the vengeance: he shall wash his feet in the blood of the wicked.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
So that a man shall say, Truly there is a reward for the righteous: truly he is a God that judges in the earth.

< Masalimo 58 >