< Masalimo 58 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
For the end. Destroy not: by David, for a memorial. If ye do indeed speak righteousness, [then] do ye judge rightly, ye sons of men.
2 Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
For ye work iniquities in [your] hearts in the earth: your hands plot unrighteousness.
3 Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
Sinners have gone astray from the womb: they go astray from the belly: they speak lies.
4 Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
Their venom is like [that] of a serpent; as [that] of a deaf asp, and that stops her ears;
5 Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
which will not hear the voice of charmers, nor [heed] the charm prepared skillfully by the wise.
6 Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
God has crushed their teeth in their mouth: God has broken the cheek-teeth of the lions.
7 Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
They shall utterly pass away like water running through: he shall bend his bow till they shall fail.
8 Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
They shall be destroyed as melted wax: the fire has fallen and they have not seen the sun.
9 Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
Before your thorns feel the white thorn, he shall swallow you up as living, as in his wrath.
10 Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
The righteous shall rejoice when he sees the vengeance of the ungodly: he shall wash his hands in the blood of the sinner.
11 Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”
And a man shall say, Verily then there is a reward for the righteous: verily there is a God that judges them in the earth.