< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Tretrezo iraho ry Andrianañahare, iferenaiño, fa Ihe ro fitsoloham-piaiko; eka! an-talinjon’ ela’o ao ty fipalirako, ampara’ te ihelaña’ ty hankàñe.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Kanjieko t’i Andrianañahare Abo-tia; Aman’ Añahare fahatafeterako.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Hahitri’e hirik’an-dikerañe ao ty fandrombahañe ahy, endaha’e i mandialia ahikoy. Selà Ho sangitrihen’ Añahare ty fiferenaiña’e naho ty hatò’e.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
An-teñateñan-diona ao ty fiaiko; itraofako handre o mpikofòke afoo; toe o ana’ ondatio, lefoñe naho ana-pale o famotsi’eo, fibara masioñe ty famele’iareo.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Onjoneñe ambone’ i likerañey irehe, ry Andrianañahare, ambone’ ty tane toy iaby ty enge’o.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Nikotepe’ iareo harato o liakoo; mibokobokoke ty fiaiko; nihalia’ iereo koboñe ty aoloko eo, f’ie nigodoñe am-po’e ao. Selà
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Mijadoñe ty troko ry Andrianañahare, eka, gañe ty troko; hisabo iraho, eka hisabo fandrengeañe.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Mivañona, ry engeko! Mitroara ry kararàke naho marovany, hampitsekafako ty fanjirik’andro!
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Hañandriañe Azo iraho ry Talè añivo’ ondatio eo, ho rengeko an-tsabo amo kilakila‘ndatio ao.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Amy te ra’elahy pak’ an-dindiñe añe ty fiferenaiña’o; le pak’an-drahoñe eñe ty hatò’o.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Onjoneñe ambonen-dikerañ’eñe irehe ry Andrianañahare, ty enge’o ambone’ ty tane bey toy.

< Masalimo 57 >