< Masalimo 57 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Ne perdez pas entièrement; par David, pour une inscription de titre, lorsqu’il s’enfuit de devant la face de Saül dans la caverne. Ayez pitié de moi, ô Dieu, ayez pitié de moi, parce que mon âme s’est confiée en vous. Et à l’ombre de vos ailes, j’espérerai jusqu’à ce que l’iniquité soit passée.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Je crierai au Dieu très haut, au Dieu qui m’a fait du bien.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Il a envoyé du ciel, et il m’a délivré: il a donné en opprobre ceux qui me foulaient aux pieds. Dieu a envoyé sa miséricorde et sa vérité,
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Et il a arraché mon âme du milieu des petits des lions: j’ai dormi tout troublé. Les fils des hommes, leurs dents sont des armes et des flèches, et leur langue un glaive acéré.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Élevez-vous au-dessus des cieux, ô Dieu, et que sur toute la terre éclate votre gloire.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Ils ont préparé un lacs pour mes pieds, et ils ont courbé mon âme. Ils ont creusé devant ma face une fosse, et ils y sont tombés.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Mon cœur est prêt, ô Dieu, mon cœur est prêt: je chanterai et je dirai un psaume.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Lève-toi, ô ma gloire, lève-toi, psaltérion, et toi, harpe: je me lèverai au point du jour.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Je vous louerai parmi les peuples. Seigneur, et je dirai un psaume en votre honneur parmi les nations.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Parce que votre miséricorde s’est élevée jusqu’aux cieux, et votre vérité jusqu’aux nues.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Soyez exalté au-dessus des cieux, ô Dieu, et que sur toute la terre éclate votre gloire.