< Masalimo 57 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Au maître de chant. « Ne détruis pas. » Hymne de David, lorsque, poursuivi par Saül, il se réfugia dans la caverne. Aie pitié de moi, ô Dieu, aie pitié de moi, car en toi mon âme cherche un refuge; je m’abriterai à l’ombre de tes ailes, jusqu’à ce que la calamité soit passée.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Je crie vers le Dieu Très-Haut, le Dieu qui fait tout pour moi.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Il m’enverra du ciel le salut: — mon persécuteur m’accable d’outrages! — Séla. Dieu enverra sa bonté et sa vérité.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Je couche au milieu des lions, des hommes qui vomissent la flamme, qui ont pour dents la lance et les flèches, et dont la langue est un glaive tranchant.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Elève-toi au-dessus des cieux, ô Dieu, que ta gloire brille par toute la terre!
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Ils avaient tendu un piège devant mes pas, déjà mon âme se courbait; ils avaient creusé une fosse devant moi: ils y sont tombés! — Séla.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Mon cœur est affermi, ô Dieu, mon cœur est affermi; je chanterai et ferai retentir de joyeux instruments.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Eveille-toi, ma gloire! Eveillez-vous, ma lyre et ma harpe! Que j’éveille l’aurore!
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Je te louerai parmi les peuples, Seigneur, je te chanterai parmi les nations.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Car ta fidélité atteint jusqu’aux cieux, et ta vérité jusqu’aux nues.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Elève-toi au-dessus des cieux, ô Dieu, que ta gloire brille sur toute la terre!