< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Pour le chef musicien. Sur l'air de « Do Not Destroy ». Un poème de David, quand il fuyait Saül, dans la grotte. Soyez miséricordieux envers moi, Dieu, soyez miséricordieux envers moi, car mon âme se réfugie en toi. Oui, à l'ombre de tes ailes, je me réfugie, jusqu'à ce que le désastre soit passé.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Je crie vers le Dieu Très Haut, à Dieu qui accomplit mes demandes pour moi.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Il enverra du ciel, et me sauvera, il réprimande celui qui me poursuit. (Selah) Dieu enverra sa bonté et sa vérité.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Mon âme est parmi les lions. Je me trouve parmi ceux qui sont incendiés, même les fils des hommes, dont les dents sont des lances et des flèches, et leur langue une épée tranchante.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Sois exalté, Dieu, au-dessus des cieux! Que ta gloire soit au-dessus de toute la terre!
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Ils ont préparé un filet pour mes pas. Mon âme s'est inclinée. Ils creusent une fosse devant moi. Ils tombent eux-mêmes au milieu de tout ça. (Selah)
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Mon cœur est inébranlable, Dieu. Mon cœur est inébranlable. Je vais chanter, oui, je vais chanter des louanges.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Réveille-toi, ma gloire! Réveille-toi, luth et harpe! Je vais réveiller l'aube.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Je te louerai, Seigneur, parmi les peuples. Je chanterai tes louanges parmi les nations.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Car ta grande bonté atteint les cieux, et votre vérité dans les cieux.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Sois exalté, Dieu, au-dessus des cieux. Que ta gloire soit sur toute la terre.

< Masalimo 57 >