< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Davidin kultainen kappale, edelläveisaajalle, ettei hän hukkunut, kuin hän Saulin edestä pakeni luolaan. Jumala, ole minulle armollinen, ole minulle armollinen; sillä sinuun minun sieluni uskaltaa, ja sinun siipeis varjon alle minä turvaan siihenasti, että ahdistukset ohitse käyvät.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Minä huudan korkeimman Jumalan tykö, sen Jumalan tykö, joka minun vaivani päälle lopun tekee.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Hän lähettää taivaasta, ja varjelee minua, ja antaa ne häpiään tulla, jotka minua tahtovat niellä ylös, (Sela) lähettäköön Jumala armonsa ja totuutensa.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Minun sieluni makaa jalopeurain keskellä, jotka ovat niinkuin tulen liekki; ihmisten lapset, joiden hampaat ovat keihäs ja nuolet, ja heidän kielensä terävä miekka.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Korota itses, Jumala, taivasten ylitse ja sinun kunnias ylitse kaiken maan.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Verkon he virittivät minun käymiseni eteen, ja minun sieluni vältti: kuopan he kaivoivat minun eteeni, ja siihen he itse lankesivat, (Sela)
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
Valmis on sydämeni, Jumala, valmis on sydämeni veisaamaan ja kiittämään.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Herää kunniani, herää psaltari ja kantele, varhain minä tahdon herätä.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Herra, sinua minä tahdon kiittää kansain seassa, ja veisata pakanain seassa.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Sillä sinun armos on suuri hamaan taivaisiin asti, ja sinun totuutes pilviin asti.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Korota itses, Jumala, taivasten ylitse, ja sinun kunnias ylitse kaiken maan.

< Masalimo 57 >