< Masalimo 57 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Unto the end. May you not destroy. Of David, with the inscription of a title, when he fled from Saul into a cave. Be merciful to me, O God, be merciful to me. For my soul trusts in you. And I will hope in the shadow of your wings, until iniquity passes away.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
I will cry out to God Most High, to God who has been kind to me.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
He sent from heaven and freed me. He has surrendered into disgrace those who trampled me. God has sent his mercy and his truth.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
And he has rescued my soul from the midst of the young lions. I slept troubled. The sons of men: their teeth are weapons and arrows, and their tongue is a sharp sword.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Be exalted above the heavens, O God, and your glory above all the earth.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
They prepared a snare for my feet, and they bowed down my soul. They dug a pit before my face, yet they have fallen into it.
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
My heart is prepared, O God, my heart is prepared. I will sing, and I will compose a psalm.
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Rise up, my glory. Rise up, psaltery and harp. I will arise in early morning.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
I will confess to you, O Lord, among the peoples. I will compose a psalm to you among the nations.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
For your mercy has been magnified, even to the heavens, and your truth, even to the clouds.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Be exalted above the heavens, O God, and your glory above all the earth.

< Masalimo 57 >