< Masalimo 56 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
För sångmästaren, efter "Den stumma duvan i fjärran"; en sång av David, når filistéerna grepo honom i Gat. Var mig nådig, o Gud, ty människor stå mig efter livet; beständigt tränga mig stridsmän.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Mina förföljare stå mig beständigt efter livet; ja, de äro många, som i högmod strida mot mig.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Men när fruktan kommer över mig, sätter jag min förtröstan på dig.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
Med Guds hjälp skall jag få prisa hans ord, på Gud förtröstar jag och skall icke frukta; vad kan det som är kött göra mig?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Beständigt förbittra de livet för mig, alla deras tankar gå ut på att skada mig.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
De rota sig samman, de lägga försåt, de vakta på mina steg, ty de stå efter mitt liv.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Skulle de räddas med all sin ondska? Nej, slå ned folken, Gud, i din vrede.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Du har räknat min flykts dagar. Samla mina tårar i din lägel; de stå ju i din bok.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Så måste då mina fiender vika tillbaka på den dag då jag ropar; det vet jag, att Gud står mig bi.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
Med Guds hjälp skall jag få prisa hans ord; med HERRENS hjälp skall jag få prisa hans ord.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
På Gud förtröstar jag och skall icke frukta; vad kunna människor göra mig?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Jag har löften att infria till dig, o Gud; jag vill betala dig lovoffer.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Ty du har räddat min själ från döden, ja, mina fötter ifrån fall, så att jag kan vandra inför Gud i de levandes ljus.