< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
Ett gyldene klenodium Davids, till att föresjunga, om den dumba dufvona ibland de främmanda, då de Philisteer grepo honom i Gath. Gud, var mig nådelig, ty menniskor vilja nedersänka mig; dagliga strida de, och tränga mig.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Mine fiender nedersänka mig dagliga ty månge strida emot mig högmodeliga.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
När jag fruktar mig, så hoppas jag uppå dig.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
Jag vill prisa Guds ord; på Gud vill jag hoppas, och intet frukta mig. Hvad skulle något kött göra mig?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Dagliga strida de emot min ord; alle deras tankar äro, att de må göra mig ondt.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
De hålla tillhopa, och vakta, och taga vara uppå mina hälar, huru de mina själ gripa måga.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Hvad de ondt göra, det är allaredo tillgifvet ( säga de ). Gud störte sådana menniskor neder utan alla nåde.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Räkna min flykt; fatta mina tårar uti din lägel; utan tvifvel räknar du dem.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Då måste mina fiender tillbakavända. När jag ropar, förmärker jag, att du min Gud äst.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
Jag vill prisa Guds ord; Herrans ord vill jag prisa.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
Uppå Gud hoppas jag, och fruktar mig intet; hvad kunna menniskor göra mig?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Jag hafver gjort dig löfte, Gud, att jag dig tacka vill.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Ty du hafver frälst mina själ ifrå döden, mina fötter ifrå fall; att jag må vandra för Gudi uti de lefvandes ljuse.

< Masalimo 56 >