< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
In finem, pro populo qui a sanctis longe factus est. David in tituli inscriptionem, cum tenuerunt eum Allophyli in Geth. [Miserere mei, Deus, quoniam conculcavit me homo; tota die impugnans, tribulavit me.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Conculcaverunt me inimici mei tota die, quoniam multi bellantes adversum me.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Ab altitudine diei timebo: ego vero in te sperabo.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
In Deo laudabo sermones meos; in Deo speravi: non timebo quid faciat mihi caro.
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Tota die verba mea execrabantur; adversum me omnes cogitationes eorum in malum.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
Inhabitabunt, et abscondent; ipsi calcaneum meum observabunt. Sicut sustinuerunt animam meam,
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
pro nihilo salvos facies illos; in ira populos confringes.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Deus, vitam meam annuntiavi tibi; posuisti lacrimas meas in conspectu tuo, sicut et in promissione tua:
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
tunc convertentur inimici mei retrorsum. In quacumque die invocavero te, ecce cognovi quoniam Deus meus es.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
In Deo laudabo verbum; in Domino laudabo sermonem.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
In Deo speravi: non timebo quid faciat mihi homo.
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
In me sunt, Deus, vota tua, quæ reddam, laudationes tibi:
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
quoniam eripuisti animam meam de morte, et pedes meos de lapsu, ut placeam coram Deo in lumine viventium.

< Masalimo 56 >