< Masalimo 56 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
«Εις τον πρώτον μουσικόν, επί Ιωνάθ-ελέμ-ρεχοκίμ, Μικτάμ του Δαβίδ, οπότε εκράτησαν αυτόν οι Φιλισταίοι εν Γαθ.» Ελέησόν με, ω Θεέ, διότι άνθρωπος χάσκει να με καταπίη· όλην την ημέραν πολεμών με καταθλίβει.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Οι εχθροί μου χάσκουσιν όλην την ημέραν να με καταπίωσι· διότι πολλοί είναι, Ύψιστε, οι πολεμούντές με.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Καθ' ην ημέραν φοβηθώ, επί σε θέλω ελπίζει·
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
εν τω Θεώ θέλω αινέσει τον λόγον αυτού· επί τον Θεόν ήλπισα· δεν θέλω φοβηθή· τι να μοι κάμη σαρξ;
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Καθ' εκάστην μεταπλάττουσι τα λόγια μου· πάντες οι διαλογισμοί αυτών είναι κατ' εμού εις κακόν.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
Συνάγονται, κρύπτονται, παραφυλάττουσι τα βήματά μου, πως να πιάσωσι την ψυχήν μου.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Θέλουσι λυτρωθή διά της ανομίας; Θεέ, εν τη οργή σου κατακρήμνισον τους λαούς.
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Συ αριθμείς τας αποπλανήσεις μου· θες τα δάκρυά μου εις την φιάλην σου· δεν είναι ταύτα εν τω βιβλίω σου;
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Τότε θέλουσιν επιστρέψει οι εχθροί μου εις τα οπίσω, καθ' ην ημέραν σε επικαλεσθώ· εξεύρω τούτο, διότι ο Θεός είναι υπέρ εμού.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
Εν τω Θεώ θέλω αινέσει τον λόγον αυτού· εν τω Κυρίω θέλω αινέσει τον λόγον αυτού.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
Επί τον Θεόν ελπίζω· δεν θέλω φοβηθή· τι να μοι κάμη άνθρωπος;
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Επάνω μου, Θεέ, είναι αι προς σε ευχαί μου· θέλω σοι αποδίδει δοξολογίας.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Διότι ελύτρωσας την ψυχήν μου εκ θανάτου, ουχί και τους πόδας μου εξ ολισθήματος, διά να περιπατώ ενώπιον του Θεού εν τω φωτί των ζώντων;