< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
Pour le peuple qui a été éloigné des saints (ou des choses saintes); par David, pour une inscription de titre, lorsque les Allophylles (étrangers) le retinrent dans Geth. Ayez pitié de moi, ô Dieu, parce qu’un homme m’a foulé aux pieds: tout le jour m’attaquant, il m’a tourmenté.
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
Mes ennemis m’ont foulé aux pieds tout le jour; parce qu’ils sont nombreux, ceux qui combattent contre moi.
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Dès la hauteur du jour, je viendrai; mais j’espérerai en vous.
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
En Dieu je louerai mes discours, en Dieu j’ai espéré; je ne craindrai pas ce que pourra me faire la chair.
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
Tout le jour ils exécraient mes paroles: c’est contre moi que toutes leurs pensées s’exerçaient au mal.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
Ils habiteront près de moi et ils se cacheront; en même temps, ils observeront mes pas. Comme ils ont attendu avec constance mon âme pour la perdre,
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Vous ne les sauverez à aucun prix: dans votre colère, vous briserez des peuples. Ô Dieu!
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Je vous ai exposé ma vie; vous avez mis mes larmes en votre présence, Comme aussi dans votre promesse.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Alors mes ennemis seront rejetés en arrière. En quelque jour que je vous aie invoqué, j’ai connu que vous êtes mon Dieu.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
En Dieu, je louerai une parole; dans le Seigneur, je louerai un discours:
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
en Dieu j’ai espéré, je ne craindrai pas ce que pourra me faire un homme.
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Je vous dois, ô Dieu, des vœux que j’acquitterai, et des louanges en votre honneur.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Parce que vous avez arraché mon âme à la mort, et mes pieds à la chute, afin que je me rende agréable devant Dieu, dans la lumière des vivants.

< Masalimo 56 >