< Masalimo 56 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
(Til sangmesteren. Al-jonat-elem-rehokim. Af David. En miktam, da filisterne greb ham i Gat.) Vær mig nådig Gud, thi Mennesker vil mig til livs, jeg trænges stadig af Stridsmænd;
2 Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
mine Fjender vil mig stadig til Livs, thi mange strider bittert imod mig!
3 Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
Når jeg gribes af Frygt, vil jeg stole på dig,
4 Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
og med Guds Hjælp skal jeg prise hans Ord. Jeg stoler på Gud, jeg frygter ikke, hvad kan Kød vel gøre mig?
5 Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
De oplægger stadig Råd imod mig, alle deres Tanker går ud på ondt.
6 Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
De flokker sig sammen, ligger på Lur, jeg har dem lige i Hælene, de står mig jo efter Livet.
7 Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
Gengæld du dem det onde, stød Folkene ned i Vrede, o Gud!
8 Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
Selv har du talt mine Suk, i din Lædersæk har du gemt mine Tårer; de står jo i din Bog.
9 Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
Da skal Fjenderne vige, den Dag jeg kalder; så meget ved jeg, at Gud er med mig.
10 Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
Med Guds Hjælp skal jeg prise hans Ord, med HERRENs Hjælp skal jeg prise hans Ord.
11 mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
Jeg stoler på Gud, jeg frygter ikke, hvad kan et Menneske gøre mig?
12 Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
Jeg har Løfter til dig at indfri, o Gud, med Takofre vil jeg betale dig.
13 Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.
Thi fra Døden frier du min Sjæl, ja min Fod fra Fald, at jeg kan vandre for Guds Åsyn i Livets Lys.

< Masalimo 56 >