< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
برای رهبر سرایندگان: با همراهی سازهای زهی. قصیدۀ داوود. خدایا، به دعای من گوش فرا ده. هنگامی که نزد تو ناله می‌کنم، خود را پنهان نکن.
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
دعایم را بشنو و آن را مستجاب فرما، زیرا از شدت پریشانی فکر، نمی‌دانم چه کنم.
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
تهدید دشمنان و ظلم بدکاران، خاطرم را آشفته کرده است. آنان با خشم و نفرت با من رفتار می‌کنند و مرا عذاب می‌دهند.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
ترس بر قلبم چنگ انداخته و مرا بی‌قرار کرده؛ وحشت مرگ سراسر وجودم را فرا گرفته است.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
از شدت ترس و لرز نزدیک است قالب تهی کنم.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
به خود می‌گویم: «ای کاش همچون کبوتر بال می‌داشتم تا به جایی دور در صحرا پرواز می‌کردم و در آنجا پنهان می‌شدم و استراحت می‌کردم؛
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
می‌شتافتم به سوی پناهگاهی و از تندباد و طوفان حوادث در امان می‌ماندم.»
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
خداوندا، این شریران را چنان پریشان کن که زبان یکدیگر را نفهمند، زیرا آنان شهر را از خشونت و ظلم پر ساخته‌اند.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
آنان روز و شب شهر را دور می‌زنند و شرارت و جنایت می‌آفرینند.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
شهر پر از ظلم و فساد است و حیله و فریب از کوچه‌ها دور نمی‌شود.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
این دشمن من نیست که به من توهین می‌کند، و گرنه تحمل می‌کردم؛ این حریف من نیست که بر من برخاسته، و گرنه خود را از او پنهان می‌کردم.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
این تو هستی ای دوست صمیمی و همکار من!
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
ما با یکدیگر رفاقت صادقانه داشتیم، با یکدیگر درد دل می‌کردیم و با هم به خانهٔ خدا می‌رفتیم.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
باشد که دشمنانم پیش از وقت، زنده به گور شوند، زیرا دلها و خانه‌هایشان پر از شرارت است. (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
اما من از خدا کمک می‌طلبم و او نجاتم خواهد داد.
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
صبح، ظهر و شب به پیشگاه خدا می‌نالم و شکایت می‌کنم و او صدای مرا خواهد شنید.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
هر چند دشمنان من زیادند، اما او مرا در جنگ با آنها پیروز خواهد ساخت و به سلامت باز خواهد گرداند.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
خدایی که از ازل بر تخت فرمانروایی نشسته است دعایم را خواهد شنید و آنها را شکست خواهد داد، زیرا آنها از خدا نمی‌ترسند و نقشه‌های پلید خود را تغییر نمی‌دهند.
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
دوست و همکار سابق من دست خود را بر روی دوستانش بلند می‌کند و عهد دوستی خود را می‌شکند.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
زبانش چرب است اما در باطنش کینه و نفرت هست. سخنانش از روغن نیز نرمتر است اما همچون شمشیر می‌برد و زخمی می‌کند.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
نگرانی خود را به خدا واگذار و او تو را حفظ خواهد کرد. خداوند هرگز نخواهد گذاشت که عادلان بلغزند و بیفتند.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
اما تو ای خدا، این اشخاص خونخوار و نیرنگ‌باز را پیش از وقت به گور خواهی فرستاد. ولی من بر تو توکل دارم.

< Masalimo 55 >