< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
`In Ebreu thus, To victorie in orguns, the lernyng of Dauid. `In Jeroms translacioun thus, To the ouercomer in salmes of Dauid lernid. God, here thou my preier, and dispise thou not my biseching;
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
yyue thou tent to me, and here thou me. I am sorewful in myn exercising; and Y am disturblid of the face of the enemye,
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
and of the tribulacioun of the synner. For thei bowiden wickidnessis in to me; and in ire thei weren diseseful to me.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
Myn herte was disturblid in me; and the drede of deth felde on me.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
Drede and trembling camen on me; and derknessis hiliden me.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
And Y seide, Who schal yyue to me fetheris, as of a culuer; and Y schal fle, and schal take rest?
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
Lo! Y yede fer awei, and fledde; and Y dwellide in wildirnesse.
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
I abood hym, that made me saaf fro the litilnesse, `ether drede, of spirit; and fro tempest.
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
Lord, caste thou doun, departe thou the tungis of hem; for Y siy wickidnesse and ayenseiyng in the citee.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
Bi dai and nyyt wickidnesse schal cumpasse it on the wallis therof;
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
and trauel and vnriytfulnesse ben in the myddis therof. And vsure and gile failide not; fro the stretis therof.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
For if myn enemye hadde cursid me; sotheli Y hadde suffride. And if he, that hatide me, hadde spoke greet thingis on me; in hap Y hadde hid me fro hym.
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
But thou art a man of o wille; my leeder, and my knowun.
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
Which tokist togidere swete meetis with me; we yeden with consent in the hous of God.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
Deth come on hem; and go thei doun quyk in to helle. For weiwardnessis ben in the dwelling places of hem; in the myddis of hem. (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
But Y criede to thee, Lord; and the Lord sauede me.
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
In the euentid and morewtid and in myddai Y schal telle, and schewe; and he schal here my vois.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
He schal ayenbie my soule in pees fro hem, that neiyen to me; for among manye thei weren with me.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
God schal here; and he that is bifore the worldis schal make hem low. For chaungyng is not to hem, and thei dredden not God;
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
he holdith forth his hoond in yelding. Thei defouliden his testament,
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
the cheris therof weren departid fro ire; and his herte neiyede. The wordis therof weren softer than oyle; and tho ben dartis.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
Caste thi cure on the Lord, and he schal fulli nurische thee; and he schal not yyue with outen ende flotering to a iust man.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
But thou, God, schalt lede hem forth; in to the pit of deth. Menquelleris and gilours schulen not haue half her daies; but, Lord, Y schal hope in thee.

< Masalimo 55 >