< Masalimo 55 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
Přednímu kantoru na neginot, vyučující žalm Davidův. Slyš, ó Bože, modlitbu mou, a neskrývej se před prosbou mou.
2 mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
Pozoruj a vyslyš mne, neboť naříkám v úpění svém, a kormoutím se,
3 chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
A to pro křik nepřítele, pro nátisk bezbožníka; neboť sčítají na mne lživé věci, a s vzteklostí se proti mně postavují.
4 Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
Srdce mé bolestí ve mně, a strachové smrti připadli na mne.
5 Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
Bázeň a strach přišel na mne, a hrůza přikvačila mne.
6 Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
I řekl jsem: Ó bych měl křídla jako holubice, zaletěl bych a poodpočinul.
7 Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
Aj, daleko bych se vzdálil, a přebýval bych na poušti. (Sélah)
8 Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
Pospíšil bych ujíti větru prudkému a vichřici.
9 Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
Zkaz je, ó Pane, změť jazyk jejich, neboť jsem spatřil bezpráví a rozbroj v městě.
10 Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
Dnem i nocí ty věci je obkličují po zdech jeho, a v prostředku jeho jest nepravost a převrácenost.
11 Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
Těžkosti jsou u prostřed něho, aniž vychází chytrost a lest z ulic jeho.
12 Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
Nebo ne nějaký nepřítel útržky mi činil, sic jinak snesl bych to; ani ten, kdož mne nenávidí, pozdvihl se proti mně, nebo skryl bych se před ním:
13 Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
Ale ty, člověče mně rovný, vůdce můj a domácí můj;
14 Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
Ješto jsme spolu mile tajné rady držívali, a do domu Božího společně chodívali.
15 Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
Ó by je smrt náhle přikvačila, tak aby za živa sstoupiti musili do pekla; nebo jest nešlechetnost v příbytcích jejich a u prostřed nich. (Sheol h7585)
16 Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
Já pak k Bohu volati budu, a Hospodin vysvobodí mne.
17 Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
U večer, i ráno, též o poledni modliti se, a nezbedně volati budu, až i vyslyší hlas můj.
18 Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
Vykoupíť duši mou, tak aby v pokoji byla před válkou proti mně; nebo veliké množství bylo jich při mně.
19 Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
Vyslyšíť Bůh silný, a je ssouží, (neboť sedí od věčnosti, (Sélah) proto že nenapravují, aniž se bojí Boha.
20 Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
Vztáhl ruce své na ty, kteříž s ním pokoj měli, a zrušil smlouvu svou.
21 Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
Libější než máslo byla slova úst jeho, ale v srdci boj; měkčejší nad olej řeči jeho, a však byly jako mečové.
22 Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
Uvrz na Hospodina břímě své, a onť opatrovati tě bude, aniž dopustí, aby na věky pohnut byl spravedlivý.
23 Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.
Ale onyno, ty Bože, svedeš do jámy zatracení; lidé zajisté vražedlní a lstiví nedojdou polovice dnů svých, já pak v tebe doufati budu.

< Masalimo 55 >