< Masalimo 54 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Скапэ-мэ, Думнезеуле, прин Нумеле Тэу ши фэ-мь дрептате прин путеря Та!
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
Аскултэ-мь ругэчуня, Думнезеуле, я аминте ла кувинтеле гурий меле!
3 Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
Кэч ниште стрэинь с-ау скулат ымпотрива мя, ниште оамень асуприторь вор сэ-мь я вяца; ей ну се гындеск ла Думнезеу.
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
Да, Думнезеу есте ажуторул меу, Домнул есте сприжинул суфлетулуй меу!
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
Рэул се ва ынтоарче асупра потривничилор мей; нимичеште-й ын крединчошия Та!
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
Атунч Ыць вой адуче жертфе де бунэвое, вой лэуда Нумеле Тэу, Доамне, кэч есте биневоитор;
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
кэч Ел мэ избэвеште дин тоате неказуриле, ши ку окий мей ымь вэд ымплинитэ доринца привитоаре ла врэжмаший мей.