< Masalimo 54 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Nkulunkulu, ngisindisa ngebizo lakho, ungahlulele ngamandla akho.
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
Nkulunkulu, zwana umkhuleko wami, ubeke indlebe emazwini omlomo wami.
3 Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
Ngoba abemzini bangivukele, abalolunya badinga umphefumulo wami, kababekanga uNkulunkulu phambi kwabo. (Sela)
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
Khangela, uNkulunkulu ungumsizi wami; iNkosi ilalabo abasekela umphefumulo wami.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
Izaphindisela ububi ezitheni zami. Baqume ngeqiniso lakho.
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
Ngizanikela umhlatshelo kuwe ngokukhululeka, ngizadumisa ibizo lakho, Nkosi, ngoba lihle.
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Ngoba ungikhulule ekuhluphekeni konke, lelihlo lami libonile isiloyiso sami ezitheni zami.

< Masalimo 54 >