< Masalimo 54 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Pour la fin dans les cantiques, intelligence à David. Lorsque les habitants de Ziph furent venus et eurent dit a Saül: Est-ce que David n’est pas chez nous? Dieu, sauvez-moi par votre nom, et jugez-moi par votre puissance.
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
Dieu, exaucez ma prière, prêtez l’oreille aux paroles de ma bouche.
3 Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
Parce que des étrangers se sont élevés contre moi, et des ennemis puissants ont cherché mon âme; ils n’ont pas mis Dieu devant leurs yeux.
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
Mais voilà que Dieu vient à mon aide; et le Seigneur est le soutien de mon âme.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
Tournez les maux du côté de mes ennemis; et par votre fidélité dans les promesses, exterminez-les.
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
Je vous offrirai, volontairement, un sacrifice; je louerai votre nom, parce qu’il est bon.
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Parce que vous m’avez retiré de toute tribulation, et que sur mes ennemis, mon œil a jeté un regard de mépris.

< Masalimo 54 >