< Masalimo 54 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Au chef des chantres. Avec instruments à cordes. Cantique de David. Lorsque les Ziphiens vinrent dire à Saül: David n’est-il pas caché parmi nous? O Dieu! Sauve-moi par ton nom, Et rends-moi justice par ta puissance!
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
O Dieu! Écoute ma prière, Prête l’oreille aux paroles de ma bouche!
3 Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
Car des étrangers se sont levés contre moi, Des hommes violents en veulent à ma vie; Ils ne portent pas leurs pensées sur Dieu. (Pause)
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
Voici, Dieu est mon secours, Le Seigneur est le soutien de mon âme.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
Le mal retombera sur mes adversaires; Anéantis-les, dans ta fidélité!
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
Je t’offrirai de bon cœur des sacrifices; Je louerai ton nom, ô Éternel! car il est favorable,
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Car il me délivre de toute détresse, Et mes yeux se réjouissent à la vue de mes ennemis.

< Masalimo 54 >