< Masalimo 54 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
To victorie in orguns, ether in salmes, the lernyng of Dauid, `whanne Zyfeys camen, and seiden to Saul, Whethir Dauid is not hid at vs? God, in thi name make thou me saaf; and in thi vertu deme thou me.
2 Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
God, here thou my preier; with eeris perseyue thou the wordis of my mouth.
3 Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
For aliens han rise ayens me, and stronge men souyten my lijf; and thei settiden not God bifor her siyt.
4 Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
For, lo! God helpith me; and the Lord is vptaker of my soule.
5 Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
Turne thou awei yuelis to myn enemyes; and leese thou hem in thi treuthe.
6 Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
Wilfuli Y schal make sacrifice to thee; and, Lord, Y schal knouleche to thi name, for it is good.
7 Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
For thou delyueridist me fro al tribulacioun; and myn iye dispiside on myn enemyes.