< Masalimo 53 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
En undervisning Davids, i chorenom ymsom till att föresjunga. De galne säga i sitt hjerta: Det är ingen Gud till; de doga intet, och äro en styggelse vordne uti deras onda väsende; ingen är som godt gör.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
Gud såg af himmelen uppå menniskors barn, att han måtte se, om der någor förståndig vore, den efter Gud frågade.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
Men de äro alle affallne, och allesammans odugelige; der är ingen, som godt gör, ja, icke en.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Vilja då de ogerningsmän icke låta säga sig, de der mitt folk fräta, på det de skola föda sig? Gud åkalla de intet.
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
Men der frukta de sig, der intet fruktande är; ty Gud förskingrar de plågares ben. Du gör dem till skam, ty Gud förmår dem.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Ack, att den hjelp utaf Zion öfver Israel komma måtte, och Gud sitt fångna folk förlöste; så skulle Jacob fröjda sig, och Israel glad vara.

< Masalimo 53 >