< Masalimo 53 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
Pour la fin, pour Maheleth. Intelligence à David. Ils se sont corrompus, et sont devenus abominables dans leurs iniquités; il n’en est pas qui fasse le bien.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
Dieu, du haut du ciel, a jeté un regard sur les fils des hommes, afin de voir s’il en est un intelligent ou cherchant Dieu.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
Tous se sont détournés, tous ensemble sont devenus inutiles; il n’en est pas qui fassent le bien; il n’en est pas même un seul.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Est-ce qu’ils ne connaîtront point, tous ceux qui opèrent l’iniquité, qui dévorent mon peuple comme un morceau de pain?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
Ils n’ont pas invoqué le Seigneur, ils ont tremblé de frayeur là où n’était pas la crainte. Parce que Dieu a dispersé les os de ceux qui plaisent aux hommes; ils ont été confondus, parce que le Seigneur les a méprisés.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Qui fera sortir de Sion le salut d’Israël? Lorsque Dieu aura ramené la captivité de son peuple, Jacob exultera: Israël sera dans l’allégresse.