< Masalimo 53 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
Jusqu'à la Fin, sur Maeleth. Une instruction de David. L'insensé a dit en son cœur: Il n'y a point de Dieu. Ils se sont corrompus; ils sont devenus abominables en iniquités, et il n'en est pas qui fasse le bien.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
Dieu, du haut du ciel, s'est penché vers les fils des hommes, pour voir s'il en est qui comprenne ou cherche Dieu.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
Tous ont dévié, et en même temps ils sont devenus inutiles; il n'en est pas qui fasse le bien, pas un seul.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Nul ne sera-t-il instruit parmi ces ouvriers d'iniquité qui dévorent mon peuple comme du pain?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
Ils n'ont point invoqué Dieu, et ils ont tremblé de peur là où il n'y avait rien à craindre. Mais Dieu a dispersé les os de ceux qui ne veulent plaire qu'aux hommes. Ils ont été confondus, parce que Dieu les a anéantis.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Qui fera sortir de Sion le salut d'Israël? Quand le Seigneur aura ramené son peuple de la captivité, Jacob tressaillira d'allégresse, et Israël sera dans la joie.