< Masalimo 53 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
[Only] foolish people say to themselves, “There is no God!” People who say that are corrupt; they commit terrible sins; there is not one of them who does what is good/right.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
God looks down from heaven and sees humans; he looks to see if anyone is [very] wise, with the result that he seeks [to know] God.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
[But] they are all morally corrupt; no one does what is good/right.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Will all these evil people never learn [what God will do to them]? They act violently toward Yahweh’s people while eating the food that he provides, and they never pray to Yahweh.
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
But [some day] those people will become terrified, like they have never been terrified before, because God will cause those who are separated from him to die, and he will [disrespect them by] scattering their bones. They have rejected God, so he will cause them to be [defeated and] completely disgraced.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
I wish/desire that someone from Jerusalem [MTY] would come and rescue the Israeli [people]! God, when you bless your people again, [all] the Israeli [people, all the descendants of] Jacob, will rejoice.

< Masalimo 53 >