< Masalimo 53 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
To the Chief Musician. On Mahalath. A Psalm of Instruction, of David. The impious hath said in his heart, There is no God! They have acted corruptly, They have wrought abominable perversity, There is none that doeth good: —
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
God, out of the heavens, looked down upon the sons of men, —To see whether there was one that showed wisdom, Enquiring after God.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
They all, have turned back, together have they become tainted, —There is none that doeth good, Not so much as, one!
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Are the workers of iniquity, without knowledge? Devouring my people, [as] they devour food? Upon God, have they not called.
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
There have they been in great dread where no dread was, Because, God, hath scattered the bones of thy besieger, —Thou hast put [him] to shame, Because, God, had, rejected, them.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Oh that, out of Zion, were granted the salvations of Israel! When God bringeth back the captives of his people, Jacob, shall exult, Israel, shall be glad.

< Masalimo 53 >