< Masalimo 53 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
Unto the end, for Maeleth, understandings to David. The fool said in his heart: There is no God. They are corrupted, and become abominable in iniquities: there is none that doth good.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
God looked down from heaven on the children of men: to see if there were any that did understand, or did seek God.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
All have gone aside, they are become unprofitable together, there is none that doth good, no not one.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Shall not all the workers of iniquity know, who eat up my people as they eat bread?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
They have not called upon God: there have they trembled for fear, where there was no fear. For God hath scattered the bones of them that please men: they have been confounded, because God hath despised them.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Who will give out of Sion the salvation of Israel? when God shall bring back the captivity of his people, Jacob shall rejoice, and Israel shall be glad.