< Masalimo 52 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
Пентру че те фэлешть ку рэутатя та, асуприторуле? Бунэтатя луй Думнезеу цине ын вечь.
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
Лимба та ну нэскочеште декыт рэутате, ка ун брич аскуцит, виклян че ешть!
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
Ту юбешть май деграбэ рэул декыт бинеле, май деграбэ минчуна декыт адевэрул.
4 Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
Ту юбешть нумай кувинте нимичитоаре, лимбэ ыншелэтоаре!
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
Де ачея ши Думнезеу те ва доборы пе вечие, те ва апука ши те ва ридика дин кортул тэу ши те ва дезрэдэчина дин пэмынтул челор вий.
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
Чей фэрэ приханэ вор ведя лукрул ачеста, се вор теме ши вор рыде де ел, зикынд:
7 “Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
„Ятэ омул каре ну луа ка окротитор пе Думнезеу, чи се ынкредя ын богэцииле луй челе марь ши се бизуя пе рэутатя луй.”
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
Дар еу сунт ын Каса луй Думнезеу ка ун мэслин верде, мэ ынкред ын бунэтатя луй Думнезеу ын вечь де вечь.
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.
Те вой лэуда тотдяуна пентру кэ ай лукрат ши, ын фаца копиилор Тэй, вой нэдэждуи ын Нумеле Тэу, кэч есте биневоитор.

< Masalimo 52 >