< Masalimo 52 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
NO ke aha la e hoonui ai oe ma ka hewa, e ke kanaka ikaika? E mau loa ana no ka lokomaikai o ke Akua.
2 Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
Ua hoomakaukau kou alelo i na mea hewa; Me he pahi umiumi la, e hana malu ana.
3 Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
Makemake no oe i ka ino, aole i ka maikai; A i ka hoopunipuni ana hoi, aole i ka olelo i ka pono. (Sila)
4 Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
Makemake no oe i na olelo a pau e pau ai, E ke alelo kumakaia.
5 Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
E hoohiolo mai no hoi ke Akua ia oe a mau loa, E kiola aku oia ia oe, a kaili aku mai loko aku o kou wahi i noho ai, A e uhuki ae hoi oia ia oe mailoko ae o ka aina o ka poe ola. (Sila)
6 Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
E ike no hoi ka poe pono, a e weliweli, A e akaaka lakou ia ia.
7 “Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
Aia hoi, oia ke kanaka i lawe ole i ke Akua i ikaika nona; Aka, ua hilinai i ka nui o kona waiwai iho, A ua hooikaika ia ia iho iloko o kona hewa.
8 Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
Aka, he mea like au me ka laauoliva uliuli iloko a ka hale o ke Akua; E hilinai mau aku wau i ke aloha o ke Akua a mau loa aku.
9 Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.
E hoolea mau loa aku au ia oe, No ka mea, nau no ia i hana; E hilinai hoi au i kou inoa; No ka mea, he pono ia imua o kou poe haipule.

< Masalimo 52 >