< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Wɔde ma dwonkyerɛfo. Dawid dwom a ɔtoo no bere a ɔde ne ho kaa Batseba na odiyifo Natan kɔɔ ne nkyɛn no. Ao, Onyankopɔn hu me mmɔbɔ, sɛnea wʼadɔe a ɛnsa da no te; wʼahummɔbɔ kɛse no nti, pepa me mmarato.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Hohoro mʼamumɔyɛ nyinaa na tew me ho fi me bɔne mu!
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Na mahu me mmarato, na mekae me bɔne daa.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Mayɛ mfomso atia wo; atia wo nko ara na mayɛ nea ɛyɛ bɔne wɔ wʼani so, enti wudi bem wɔ wʼatemmu mu na woteɛ wɔ wʼatemmu mu.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Ampa ara wɔwoo me wɔ bɔne mu, na bɔne mu na me na nyinsɛn me.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Ampa ara nokware na wohwehwɛ wɔ me mu. Wokyerɛ me nyansa a mu dɔ.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Fa adwerɛ hohoro me ho, na me ho afi; guare me, na mɛhoa asen sukyerɛmma.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Ma mente ahosɛpɛw ne anigye nka; na ma nnompe a woabubu no nni ahurusi.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Kata wʼani wɔ me bɔne ho na pepa mʼamumɔyɛ nyinaa.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Ao, Onyankopɔn, bɔ koma a mu tew wɔ me mu, na yɛ honhom a atim no foforo wɔ me mu.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Mpam me mfi wʼanim, na nyi wo Honhom Kronkron mfi me mu.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Fa wo nkwagye mu anigye no ma me bio, na ma me ɔpɛ honhom a ɛbɛma magyina.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Afei mɛkyerɛ nnebɔneyɛfo wʼakwan, na amumɔyɛfo bɛsan aba wo nkyɛn.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Ao, Onyankopɔn, gye me fi mogya ho afɔdi mu. Onyame a wugye me nkwa, na me tɛkrɛma bɛto wo trenee ho dwom.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Awurade, bue mʼano fafa, na mede mʼano bɛpae mu aka wʼayeyi.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Wompɛ afɔrebɔ, anka mɛbɔ; wʼani nnye ɔhyew afɔre ho.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Onyankopɔn afɔre yɛ honhom a abotow, Onyankopɔn, worempo ahonu ne ahobrɛase koma.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Ma ɛnyɛ wo fɛ sɛ wobɛma Sion anya nkɔso wɔ wʼanigye mu; na woasi Yerusalem afasu.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Afei wʼani begye ɔtreneeni afɔrebɔ ho, ɔhyew afɔre a edi mu; na wɔde anantwinini bɛbɔ afɔre wʼafɔremuka so.

< Masalimo 51 >