< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
För sångmästaren; en psalm av David, när profeten Natan kom till honom, då han hade gått in till Bat-Seba. Gud, var mig nådig efter din godhet, utplåna mina överträdelser efter din stora barmhärtighet.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Två mig väl från min missgärning, och rena mig från synd.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Ty jag känner mina överträdelser, och min synd är alltid inför mig.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Mot dig allena har jag syndat och gjort vad ont är i dina ögon; på det att du må finnas rättfärdig i dina ord och rättvis i dina domar.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Se, i synd är jag född, och i synd har min moder avlat mig.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Du har ju behag till sanning i hjärtegrunden; så lär mig då vishet i mitt innersta.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Skära mig med isop, så att jag varder ren; två mig, så att jag bliver vitare än snö.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Låt mig förnimma fröjd och glädje, låt de ben som du har krossat få fröjda sig.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Vänd bort ditt ansikte från mina synder, och utplåna alla mina missgärningar.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Skapa i mig, Gud, ett rent hjärta, och giv mig på nytt en frimodig ande.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Förkasta mig icke från ditt ansikte, och tag icke din helige Ande ifrån mig.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Låt mig åter få fröjdas över din frälsning, och uppehåll mig med villighetens ande.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Då skall jag lära överträdarna dina vägar, och syndarna skola omvända sig till dig.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Rädda mig undan blodstider, Gud, du min frälsnings Gud, så skall min tunga jubla över din rättfärdighet.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Herre, upplåt mina läppar, så att min mun kan förkunna ditt lov.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Ty du har icke behag till offer, eljest skulle jag giva dig sådana; till brännoffer har du icke lust.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Det offer som behagar Gud är en förkrossad ande; ett förkrossat och bedrövat hjärta skall du, Gud, icke förakta.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Gör väl mot Sion i din nåd, bygg upp Jerusalems murar.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Då skall du undfå rätta offer, som behaga dig, brännoffer och heloffer; då skall man offra tjurar på ditt altare.

< Masalimo 51 >