< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
in finem psalmus David cum venit ad eum Nathan propheta quando intravit ad Bethsabee miserere mei Deus secundum magnam misericordiam tuam et secundum multitudinem miserationum tuarum dele iniquitatem meam
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
amplius lava me ab iniquitate mea et a peccato meo munda me
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
quoniam iniquitatem meam ego cognosco et peccatum meum contra me est semper
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
tibi soli peccavi et malum coram te feci ut iustificeris in sermonibus tuis et vincas cum iudicaris
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
ecce enim in iniquitatibus conceptus sum et in peccatis concepit me mater mea
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
ecce enim veritatem dilexisti incerta et occulta sapientiae tuae manifestasti mihi
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
asparges me hysopo et mundabor lavabis me et super nivem dealbabor
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
auditui meo dabis gaudium et laetitiam exultabunt ossa humiliata
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
averte faciem tuam a peccatis meis et omnes iniquitates meas dele
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
cor mundum crea in me Deus et spiritum rectum innova in visceribus meis
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
ne proicias me a facie tua et spiritum sanctum tuum ne auferas a me
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
redde mihi laetitiam salutaris tui et spiritu principali confirma me
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
docebo iniquos vias tuas et impii ad te convertentur
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
libera me de sanguinibus Deus Deus salutis meae exultabit lingua mea iustitiam tuam
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Domine labia mea aperies et os meum adnuntiabit laudem tuam
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
quoniam si voluisses sacrificium dedissem utique holocaustis non delectaberis
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
sacrificium Deo spiritus contribulatus cor contritum et humiliatum Deus non spernet
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
benigne fac Domine in bona voluntate tua Sion et aedificentur muri Hierusalem
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
tunc acceptabis sacrificium iustitiae oblationes et holocausta tunc inponent super altare tuum vitulos

< Masalimo 51 >