< Masalimo 51 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Kaasianak, O Dios, gapu iti kinapudnom; gapu iti kinawadwad ti kaasim, punasem dagiti nagbasolak.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Ugasannak a naan-anay manipud iti kinadakesko ken dalusannak iti nagbasolak.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Ta ammok dagiti nagbasolak, ken adda a kanayon iti sangoanak ti basolko.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Nagbasolak kenka, sika laeng ti nagbasolak ken nagaramidak ti dakes iti imatangmo; hustoka tunggal agsaoka; nalinteg iti panangukommo.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Kitaem, naiyanakak iti kinadakes; sipud pay inyinawnak ti inak, nagbasolakon.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Kitaem, tarigagayam ti kinapudno iti pusok; iti pusok impakaammom kaniak ti kinasirib.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Pasin-awennak babaen iti hisopo, ket dumalusakto; ugasannak, ket napudpudawakto ngem iti niebe.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Ipangngegmo kaniak ti rag-o ken ragsak tapno agrag-oda dagiti tulang a tinukkolmo.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Ilemmengmo ti rupam manipud kadagiti basolko ken punasem amin dagiti kinadakesko.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Parsuaem kaniak, O Dios, ti nadalus a puso ken ikkannak iti baro ken napudno nga espiritu.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Saannak a papanawen iti imatangmo, ken dimo ipanaw kaniak ti Espiritu Santom.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Isublim kaniak ti ragsak iti panangisalakanmo, ken ikkannak iti natulnog nga espiritu.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Ket isurokto dagiti bilinmo kadagiti managbasol, ken agsublidanto kenka.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Pakawanennak gapu iti nagayus a dara, O Dios iti pannakaisalakanko, ken ipukkawkonto ti rag-o ti kinalintegmo.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
O Apo, luktam ti bibigko, ken ibalikas ti ngiwatko iti pannakaidaydayawmo.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Dimo kayat dagiti daton a sacrificio, ta no kayatmo koma, isuda ti idatonko; dika met maay-ayo iti daton a maipuor.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Dagiti daton iti Dios ket dagiti napakumbaba nga espiritu. Sika, O Dios, ti saanto a mangumsi iti napakumbaba ken nagbabawi a puso.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Kaasiam ti Sion ket tulongam; bangonem manen dagiti bakud ti Jerusalem.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Ket maragsakankanto kadagiti daton iti kinalinteg, kadagiti daton a maipuor ken kadagiti daton a maipuor amin; kalpasanna, mangidatonto dagiti tattaomi kadagiti kalakian a baka iti rabaw ti altarmo.