< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
למנצח מזמור לדוד ב בבוא-אליו נתן הנביא-- כאשר-בא אל-בת-שבע ג חנני אלהים כחסדך כרב רחמיך מחה פשעי
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
הרבה (הרב) כבסני מעוני ומחטאתי טהרני
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
כי-פשעי אני אדע וחטאתי נגדי תמיד
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
לך לבדך חטאתי והרע בעיניך עשיתי למען תצדק בדברך-- תזכה בשפטך
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
הן-בעוון חוללתי ובחטא יחמתני אמי
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
הן-אמת חפצת בטחות ובסתם חכמה תודיעני
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
תחטאני באזוב ואטהר תכבסני ומשלג אלבין
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
תשמיעני ששון ושמחה תגלנה עצמות דכית
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
הסתר פניך מחטאי וכל-עונתי מחה
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
לב טהור ברא-לי אלהים ורוח נכון חדש בקרבי
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
אל-תשליכני מלפניך ורוח קדשך אל-תקח ממני
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
השיבה לי ששון ישעך ורוח נדיבה תסמכני
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
אלמדה פשעים דרכיך וחטאים אליך ישובו
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
הצילני מדמים אלהים-- אלהי תשועתי תרנן לשוני צדקתך
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
אדני שפתי תפתח ופי יגיד תהלתך
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
כי לא-תחפץ זבח ואתנה עולה לא תרצה
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
זבחי אלהים רוח נשברה לב-נשבר ונדכה-- אלהים לא תבזה
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
היטיבה ברצונך את-ציון תבנה חומות ירושלם
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
אז תחפץ זבחי-צדק עולה וכליל אז יעלו על-מזבחך פרים

< Masalimo 51 >