< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Pour le chef musicien. Psaume de David, lorsque le prophète Nathan vint le trouver, après qu'il se fut rendu à Bethsabée. Aie pitié de moi, Dieu, selon ta bonté. Selon la multitude de vos tendres miséricordes, effacez mes transgressions.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Lave-moi complètement de mon iniquité. Purifie-moi de mes péchés.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Car je connais mes transgressions. Mon péché est constamment devant moi.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Contre toi, et toi seul, j'ai péché, et fait ce qui est mauvais à tes yeux, pour que vous puissiez avoir raison quand vous parlez, et justifié quand vous jugez.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Voici, je suis né dans l'iniquité. Ma mère m'a conçu dans le péché.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Voici, vous désirez la vérité dans les parties intérieures. Tu m'enseignes la sagesse au plus profond de moi-même.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Purifie-moi avec l'hysope, et je serai pur. Lave-moi, et je serai plus blanc que neige.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Que j'entende la joie et l'allégresse, pour que les os que tu as brisés puissent se réjouir.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Cachez votre visage de mes péchés, et efface toutes mes iniquités.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Crée en moi un cœur pur, ô Dieu. Renouvelez un esprit droit en moi.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Ne me rejette pas loin de ta présence, et ne m'enlève pas ton Saint Esprit.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Rends-moi la joie de ton salut. Soutiens-moi avec un esprit volontaire.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Alors j'enseignerai tes voies aux transgresseurs. Les pécheurs se convertiront à vous.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Délivre-moi de la culpabilité du sang versé, ô Dieu, le Dieu de mon salut. Ma langue chantera à haute voix ta justice.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Seigneur, ouvre mes lèvres. Ma bouche publiera tes louanges.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Car tu ne prends pas plaisir aux sacrifices, sinon je les donnerais. Tu ne prends pas plaisir à l'holocauste.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Les sacrifices de Dieu, c'est un esprit brisé. O Dieu, tu ne méprises pas un cœur brisé et contrit.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Fais bien, selon ton bon plaisir, à Sion. Construisez les murs de Jérusalem.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Alors tu prendras plaisir aux sacrifices de la justice, en holocaustes et en holocaustes entiers. Puis ils offriront des taureaux sur ton autel.

< Masalimo 51 >