< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Unto the end, a psalm of David, When Nathan the prophet came to him after he had sinned with Bethsabee. Have mercy on me, O God, according to thy great mercy. And according to the multitude of thy tender mercies blot out my iniquity.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Wash me yet more from my iniquity, and cleanse me from my sin.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
For I know my iniquity, and my sin is always before me.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
To thee only have I sinned, and have done evil before thee: that thou mayst be justified in thy words and mayst overcome when thou art judged.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
For behold I was conceived in iniquities; and in sins did my mother conceive me.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
For behold thou hast loved truth: the uncertain and hidden things of thy wisdom thou hast made manifest to me.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Thou shalt sprinkle me with hyssop, and I shall be cleansed: thou shalt wash me, and I shall be made whiter than snow.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
To my hearing thou shalt give joy and gladness: and the bones that have been humbled shall rejoice.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Turn away thy face from my sins, and blot out all my iniquities.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Create a clean heart in me, O God: and renew a right spirit within my bowels.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Cast me not away from thy face; and take not thy holy spirit from me.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Restore unto me the joy of thy salvation, and strengthen me with a perfect spirit.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
I will teach the unjust thy ways: and the wicked shall be converted to thee.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Deliver me from blood, O God, thou God of my salvation: and my tongue shall extol thy justice.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
O Lord, thou wilt open my lips: and my mouth shall declare thy praise.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
For if thou hadst desired sacrifice, I would indeed have given it: with burnt offerings thou wilt not be delighted.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
A sacrifice to God is an afflicted spirit: a contrite and humbled heart, O God, thou wilt not despise.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Deal favourably, O Lord, in thy good will with Sion; that the walls of Jerusalem may be built up.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Then shalt thou accept the sacrifice of justice, oblations and whole burnt offerings: then shall they lay calves upon thy altar.

< Masalimo 51 >