< Masalimo 50 >
1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
En salme av Asaf. Den Allmektige, Gud Herren, taler og kaller på jorden fra solens opgang til dens nedgang.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Fra Sion, skjønnhetens krone, stråler Gud frem.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Vår Gud kommer og skal ikke tie; ild fortærer for hans åsyn, og omkring ham stormer det sterkt.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Han kaller på himmelen der oppe og på jorden for å dømme sitt folk:
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Samle til mig mine fromme, som har inngått pakt med mig om offer!
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Og himmelen kunngjør hans rettferdighet; for Gud er den som skal dømme. (Sela)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Hør, mitt folk, jeg vil tale, Israel, jeg vil vidne for dig: Gud, din Gud, er jeg.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Ikke for dine offers skyld vil jeg straffe dig; dine brennoffer er alltid for mig.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Jeg vil ikke ta okser fra ditt hus eller bukker fra dine hegn.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
For mig hører alle dyr i skogen til, dyrene på fjellene i tusentall.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Jeg kjenner alle fjellenes fugler, og det som rører sig på marken, står for mig.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Om jeg hungret, vilde jeg ikke si det til dig; for mig hører jorderike til og alt det som fyller det.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Mon jeg skulde ete oksers kjøtt og drikke bukkers blod?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Ofre Gud takksigelse og gi den Høieste det du har lovt,
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
og kall på mig på nødens dag, så vil jeg utfri dig, og du skal prise mig.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
Men til den ugudelige sier Gud: Hvad har du med å fortelle om mine lover og føre min pakt i din munn?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Du hater jo tukt og kaster mine ord bak dig.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Når du ser en tyv, er du gjerne med ham, og med horkarler gjør du felles sak.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Din munn slipper du løs med ondt, og din tunge spinner sammen svik.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Du sitter og taler imot din bror, du baktaler din mors sønn.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Dette har du gjort, og jeg har tidd; du tenkte jeg var som du; men jeg vil straffe dig og stille det frem for dine øine.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Legg merke til dette, I som glemmer Gud, forat jeg ikke skal sønderrive, og det er ingen som redder!
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Den som ofrer takksigelse, ærer mig, og den som går den rette vei, ham vil jeg la skue Guds frelse.