< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Psalmus Asaph. Deus deorum Dominus locutus est: et vocavit terram, A solis ortu usque ad occasum:
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
ex Sion species decoris eius.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Deus manifeste veniet: Deus noster et non silebit. Ignis in conspectu eius exardescet: et in circuitu eius tempestas valida.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Advocavit caelum desursum: et terram discernere populum suum.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Congregate illi sanctos eius: qui ordinant testamentum eius super sacrificia.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Et annunciabunt caeli iustitiam eius: quoniam Deus iudex est.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Audi populus meus, et loquar Israel, et testificabor tibi: Deus Deus tuus ego sum.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Non in sacrificiis tuis arguam te: holocausta autem tua in conspectu meo sunt semper.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Non accipiam de domo tua vitulos: neque de gregibus tuis hircos.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
Quoniam meae sunt omnes ferae silvarum, iumenta in montibus et boves.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Cognovi omnia volatilia caeli: et pulchritudo agri mecum est.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Si esuriero, non dicam tibi: meus est enim orbis terrae, et plenitudo eius.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Numquid manducabo carnes taurorum? aut sanguinem hircorum potabo?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Immola Deo sacrificium laudis: et redde Altissimo vota tua.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Et invoca me in die tribulationis: eruam te, et honorificabis me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
Peccatori autem dixit Deus: Quare tu enarras iustitias meas, et assumis testamentum meum per os tuum?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Tu vero odisti disciplinam: et proiecisti sermones meos retrorsum:
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Si videbas furem, currebas cum eo: et cum adulteris portionem tuam ponebas.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Os tuum abundavit malitia: et lingua tua concinnabat dolos.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Sedens adversus fratrem tuum loquebaris, et adversus filium matris tuae ponebas scandalum:
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
haec fecisti, et tacui. Existimasti inique quod ero tui similis: arguam te, et statuam contra faciem tuam.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Intelligite haec qui obliviscimini Deum: nequando rapiat, et non sit qui eripiat.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Sacrificium laudis honorificabit me: et illic iter, quo ostendam illi salutare Dei.

< Masalimo 50 >