< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Drottinn er alvaldur Guð. Hann kallar þjóð sína saman úr austri og vestri.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Dýrð Guðs ljómar frá musteri hans á Síonfjalli.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Hann birtist í þrumugný, umlukinn eyðandi eldi og stormviðri.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Hann er kominn til að dæma lýð sinn. Hróp hans heyrist á himni og jörðu:
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
„Safnið saman þjóð minni sem með fórnunum á altari mínu hefur gert sáttmála við mig.“
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Guð mun dæma réttláta dóma. Himinninn vitnar um réttlæti hans.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Hlusta þú, þjóð mín! Ég er þinn Guð! Taktu eftir úrskurði mínum:
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Fórnir þínar tek ég gildar. Þar hefur þú sýnt trúfesti.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
En ég girnist þó ekki uxa þína og geitur,
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
því að öll dýr jarðarinnar tilheyra mér!
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Hjarðirnar á fjöllunum og fuglar loftsins – allt er það mitt.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Væri ég hungraður, segði ég þér ekki frá því – allt á jörðu er mitt, ekkert er undan skilið.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Nei, ég þrái ekki kjötfórnir þínar og blóðfórnir,
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
heldur þakklæti og orðheldni.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Ákallaðu mig á degi neyðarinnar og þá mun ég frelsa þig. Og þú skalt vegsama mig. Já, þetta skaltu gera.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
En við hina óguðlegu segir Drottinn: „Hættið að þylja upp lögmál mitt og heimta af mér,
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
þið sem hafnið aga og lítilsvirðið boðorð mín.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Þið aðstoðið þjófinn og samneytið hórkörlum.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Þið bölvið og ljúgið
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
og baktalið bróður ykkar.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Þannig ferst ykkur og svo á ég að þegja?! Er ég þá eins og þið? Nei, ég mun hegna ykkur svo ekki verður um villst.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
En þið sem gleymduð Guði, fáið eitt tækifæri enn, síðan læt ég eyðinguna koma og þá er allt um seinan.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Sá sem færir þakkargjörð að fórn, heiðrar mig. Og þeir sem breyta eftir orðum mínum fá að sjá hjálpræði mitt.“

< Masalimo 50 >