< Masalimo 50 >
1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Psaume d’Asaph.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
C’est de Sion que vient l’éclat de sa splendeur.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Dieu viendra manifestement: notre Dieu viendra, et il ne gardera pas le silence.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
D’en haut il appellera le ciel et la terre pour juger son peuple.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Rassemblez-lui ses saints, qui exécutent son alliance sur les sacrifices.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Et les cieux annonceront sa justice, parce que c’est Dieu lui-même qui est juge.
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Écoute, mon peuple, et je parlerai; Israël, écoute; car je te prendrai à témoin: Dieu, ton Dieu, c’est moi qui le suis.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Je ne te reprendrai pas pour tes sacrifices; car tes holocaustes sont toujours en ma présence.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Je ne prendrai pas des veaux de ta maison, ni des boucs de tes troupeaux.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
Parce qu’à moi sont toutes les bêtes des forêts, les animaux qui paissent sur les montagnes et les bœufs.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Je connais tous les volatiles du ciel, et la beauté des champs est en mon pouvoir.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Si j’ai faim, je ne te le dirai pas: car à moi est le globe de la terre, et sa plénitude.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Est-ce que je mangerai des chairs de taureaux? ou boirai-je du sang des boucs?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Immole à Dieu un sacrifice de louange, et rends au Très-Haut tes vœux.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Et invoque-moi, au jour de la tribulation: je te délivrerai, et tu m’honoreras.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
Mais au pécheur Dieu a dit: Pourquoi racontes-tu mes justices, et pourquoi ta bouche annonce-t-elle mon alliance?
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Pour toi, tu hais la discipline, et tu as rejeté ma parole derrière toi.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Si tu voyais un voleur, tu courais avec lui, et c’est avec les adultères que tu mettais ta part.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Ta bouche a abondé en malice, et ta langue ajustait des fourberies.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Assis, tu parlais contre ton frère et contre le fils de ta mère, tu posais une pierre d’achoppement.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Tu as fait ces choses, et je me suis tu.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Comprenez ces choses, vous qui oubliez Dieu; de peur qu’un jour il ne vous enlève, et qu’il n’y ait personne qui vous délivre.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
C’est un sacrifice de louange qui m’honorera; et c’est là le chemin par lequel je lui montrerai le salut de Dieu.