< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
Psaume d'Asaph Le [Dieu] Fort, le Dieu, l'Eternel a parlé, et il a appelé toute la terre, depuis le soleil levant jusques au soleil couchant.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
Dieu a fait luire sa splendeur de Sion, qui est d'une beauté parfaite.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Notre Dieu viendra, il ne se taira point: il y aura devant lui un feu dévorant, et tout autour de lui une grosse tempête.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
Il appellera les cieux d'en haut, et la terre, pour juger son peuple, [en disant]:
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
Assemblez-moi mes bien-aimés qui ont traité alliance avec moi sur le sacrifice.
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
Les cieux aussi annonceront sa justice: parce que Dieu est le juge; (Sélah)
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
Ecoute, ô mon peuple, et je parlerai; [entends], Israël, et je te sommerai; je suis Dieu, ton Dieu, moi.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
Je ne te reprendrai point pour tes sacrifices, ni pour tes holocaustes, qui ont été continuellement devant moi.
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
Je ne prendrai point de veau de ta maison, ni de boucs de tes parcs.
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
Car toute bête de la forêt est à moi, [et] les bêtes aussi qui paissent en mille montagnes.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
Je connais tous les oiseaux des montagnes; et toute sorte de bêtes des champs est à mon commandement.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
Si j'avais faim, je ne t'en dirais rien; car la terre habitable est à moi, et tout ce qui est en elle.
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
Mangerais-je la chair des gros taureaux? et boirais-je le sang des boucs?
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
Sacrifie louange à Dieu, et rends tes vœux au Souverain.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
Et invoque-moi au jour de ta détresse, je t'en tirerai hors, et tu me glorifieras.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
Mais Dieu a dit au méchant: qu'as-tu que faire de réciter mes statuts, et de prendre mon alliance en ta bouche;
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
Vu que tu hais la correction, et que tu as jeté mes paroles derrière toi?
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Si tu vois un larron, tu cours avec lui; et ta portion est avec les adultères.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
Tu lâches ta bouche au mal, et par ta langue tu trames la fraude;
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
Tu t'assieds [et] parles contre ton frère, [et] tu couvres d'opprobre le fils de ta mère.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
Tu as fait ces choses-là, et je m'en suis tu; [et] tu as estimé que véritablement je fusse comme toi; [mais] je t'en reprendrai, et je déduirai [le tout] par ordre en ta présence.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
Entendez cela maintenant, vous qui oubliez Dieu; de peur que je ne vous ravisse, et qu'il n'y ait personne qui vous délivre.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
Celui qui sacrifie la louange me glorifiera; et à celui qui prend garde à sa voie, je montrerai la délivrance de Dieu.

< Masalimo 50 >