< Masalimo 50 >

1 Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
God, the all-powerful one, speaks; he summons all people, from the east to the west.
2 Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
His glory shines from Zion [Hill in Jerusalem], an extremely beautiful city.
3 Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
Our God comes to us, and he is not silent. A great fire is in front of him, and a storm is around him.
4 Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
He comes to judge his people. He shouts to the [angels in] heaven and to [the people on] the earth.
5 Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
He says, “Summon those who faithfully [worship] me, those who made an agreement with me by offering sacrifices to me.”
6 Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
The [angels in] heaven declare, “God is righteous, and he is the supreme judge.”
7 Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
God says, “My people, listen! You Israeli people, listen, as I, your God, say what you have done that is wrong.
8 Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
I am not rebuking you for making sacrifices to me, for the offerings that you completely burn [on the altar].
9 Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
But I do not really need [you to sacrifice] the bulls from your barns and the goats from your pens,
10 pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
because all the animals in the forest belong to me, [and all] the cattle on 1,000 hills also belong to me.
11 Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
I [own and] know all the birds and all [the creatures] that move around in the fields.
12 Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
[So], if I were hungry, I would not tell you [to bring me some food], because everything in the world belongs to me!
13 Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
I do not eat the flesh of the bulls [that you sacrifice], and I do not drink the blood of the goats [that you offer to me].
14 “Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
The sacrifice [that I really want is that] you thank me and do all that you have promised to do.
15 Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
And pray to me when you have troubles. [If you do that], I will rescue you, and [then] you will praise me.
16 Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
But I say this to the wicked people: (Why do you/It does not benefit you at all to) [RHQ] recite my commandments or talk about the agreement that I made with you,
17 Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
because you have refused to allow me to discipline you, and you have rejected what I told you to do.
18 Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
Every time that you see a thief, you become his friend, and you spend [much] time with those who commit adultery.
19 Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
You are [always] talking [MTY] about doing wicked things, and you are [always] to deceive people.
20 Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
You are always accusing members of your own family [of doing wrong], and slandering them.
21 Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
You did [all] those things, and I did not say anything to you, [so] you thought that I was [a sinner] just like you. But now I rebuke you and accuse you, right in front of you.
22 “Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
So, all you who have ignored me, pay attention to this, because if you do not, I will tear you to pieces, and there will be no one to rescue you.
23 Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”
The sacrifice that [truly] honors me is to thank me [for what I have done]; and I will save those who always do the things that I want them to.”

< Masalimo 50 >